KOSI YOPHUNZITSA BAIBULO YA MA CHRISTADELPHIAN â¢^â¢^ Na. 2
KODI MA CHRISTADELPHIANS NDI NDANI?
Kuwerenga : Yohane 15
Cholinga cha kosi ya Baibuloyi ndi kuthandiza anthu kuphunzira Malemba. Komabe, mwina mungadabwe kuti, kodi ma Christadelphians ndi ndani? Choncho munkhani ino tikufotokozerani pangâono zokhudza ifeyo.
Ma Christadelphians ndi gulu la amuna ndi akazi amene akupezeka padziko lonse, amene amawerenga Baibulo lonse ndipo amaliona kuti ndi Mawu a Mulungu ouziridwa. Amakhulupirira malonjezo onse onena za Ambuye Yesu Khristu komanso onena za dziko la mâtsogolo, amene ali mâChipangano Chakale ndi Chipangano Chatsopano. Ma Christadelphians akuyembekezera kuti Yesu adzabweranso kuchokera kumwamba kuti adzakhazikitse ufumu wa Mulungu padziko lapansili.
Dzina lakuti Christadelphian anachokera kumawu awiri achigiriki, amene amatanthauza Abale mwa Khristu.
Kodi ma Christadelphians amakhala kuti?
Ma Christadelphians akupezeka mâmayiko oposa 50. Amapezeka ku Britain komanso mâmayiko ambiri a ku Ulaya. Amapezekanso mâmayiko ambirimbiri ku Africa; ku Far East, kuchokera ku India mâpaka ku Indonesia; ku Australasia ndi kuzilumba za panyanja ya Pacific. Akupezekanso mâmayko a ku North ndi South America kuchokera ku Canada mpaka kukafika ku Argentina, komanso pazilumba za ku Caribbean. Mâgululi muli amuna ndi akazi a mitundu yosiyanasiyana komanso a zikhalidwe zosiyana siyana.
Kosi iwo amakhulupirira zotani?
Chikhulupiriro cha ma Christadelphians chagona pa zinthu zimene Yesu ndi ophunzira ake ankakhupirira komanso kuphunzitsa zaka pafupifupi 2000 zapitazo. Uthenga weniweni wa Chikhristu sunasithe. Koma nâzomvetsa chisoni kuti kwa zaka mahandiredi ambirimbiri matchalitci âAchikhristuâ akhala akutsatira komanso kuphunzitsa zinthu zimene zinachokera ku zipembedzo zonyenga. Ngakhale zili choncho, padzikoli pakhala pakupezeka kagulu ka anthu ochepa kwambiri amene sanasiye kutsatira choonadi. Mwachitsazon, ku Ulaya zaka zoposa 400 zapitazo kunali anthu ambiri amene anaphunzira uthenga woona wabwino chifukwa choti ankawerenga Baibulo pawokha pamene Baibulolo linasindikizidwa mâzinenero za anthuwo. Amuna ndi akazi amenewa anayamba kutchedwa "Abale mwa Khristu". Koma nâzomvetsa chisoni kuti ambiri mwa anthu amenewa anazunzidwa koopsa, ndipo ena anaphedwa chifukwa cha chikhulupiriro chawo. Ambiri anathawa mânyumba zawo, koma pamene ankathawa anatenga Uthenga Wabwino nâkumaufalitsa mâmayiko ambiri a ku Ulaya, kuwoloka nyanja zikuluzikulu. Koma sipanapite nthawi yaitali kuti choonadicho chisakanikiranenso ndi ziphunzitso zonyenga. (Pali phunziro la mphamvu apa: Choonadi sichisokonezedwa pokhapokha ngati anthu amene ali ndi choonadiwo akuwerenga ndi kuphunzira Mawu a Mulungu pawokha.)
Kosi gulu la ma Christadelphian linayamba bwanji?
Mâchaka cha 1832, dokotala wina wa ku England, dzina lake John Thomas, amenenso anali mâbusa wa tchalitchi chinachake, anakwera sitima yapamadzi imene inkapita ku New York. Iye anachita izi chifukwa bambo ake ankafuna kusamukira ku America. Ulendowu uli mkati, sitimayo inawomba nthaka chifukwa cha namondwe woopsa amene anachitika panyanjayo, ndipo Dr. Thomas ankangoganiza kuti basi, afera pomwepo. Iye anazindikira kuti sankadziwa zambiri zokhudza tsogolo, ndipo analumbira kuti ngati safa komanso akafika kumtunda ali wabwinobwino, ndiye kuti sapuma koma nthawi yomweyo adzayamba kufufuza choonadi pa nkhani yokhudza moyo umene anthu angakhale nawo pambuyo pomwalira. Nâzosangalatsa kuti mkuluyu sanafe ndipo anafikadi ku New York. Atangofika, iye anachitadi zimene analonejza zija. Anakhala masiku okwana 15 akuphunzira Baibulo mwakhama zedi
Ndipo analinso ndi mpata wounika zimene matchalitchi ambirimbiri "Achikhristu" amaphunzitsa. Atakhutira kuti wamvetsa bwino zinthu zimene zinalembedwa mâChipangano Chakale ndi Chatsopano chomwe zokhudza Yesu Khristu komanso zokhudza kubwera kwa ufumu wa Mulungu padziko lapansi, anakonza zoti abatizidwe, thupi lonse limire mâmadzi. Iye anapitiriza kulalikira mâmadera osiyanasiyana ku America komanso ku Britain ndipo analemba magazini ndi mabuku ambirimbiri a nkhani za mawu a Mulungu.
Pa gulu la anthu amene anayamba kukhulupirira zinthu zofanana ndi John Thomas nâkuyamba kugwirizana naye pa ntchito yakeyi panali Robert Roberts, yemwe kwawo kunali ku Scotland. Roberts anathandiza pa nthawi yokonza dongosolo labwino pakati pa Akhristu a agululi amene anayamba kuchuluka kwambiri, ndipo magulu amene ankaikamo anthuwa ankawatchula kuti ma eklesia. "Eklesia" ndi mawu a mâBaibulo amene amatanthauza "msonkhano wa anthu amene aitanidwa". Ma Christadelphians amaona kuti ndi bwino kugwiritsa ntchito mawu amenewa kusiyana ndi "tchalitchi"âdzina lomwe nthawi zina limatanthauza nyumba imene anthu amapemphereramo mâmalo mwa anthu amene akupemphera mânyumbayo.
Anthu amene angomva dzinali kwa nthawi yoyamba akhoza kudabwa
Dzina lakuti Christadelphian linagwiritsidwa ntchito koyamba mu 1864 pamene anthu okhulupirira anapempha boma la America kuti asamalembedwe ntchito za usilikali pa nthawi imene ku America kunali nkhondo ya pachiweniweni. Popeza pamafunika dzina loti anthuwa azidziwika nalo, John Thomas anakumbukira "Abale mwa Khristu" amene anali zaka zoposa 300 mâmbuyomo, choncho anasankha dzina lakuti ma 'Christadelphian', lomwe ndi dzina lachigiriki otanthauza Abale mwa Khristu. Ma Christadelphians a mâzaka za ma 1800 amene ankayenda zedi nâkumalalikira uthenga mâmayiko osiyanasiyana padziko lapansili. Choncho pofika kumapeta kwa zaka za mâma 1800, anthuwa anali akupezeka mâmayiko ambirimbiri padziko lonse.
Kodi gulu la ma Christadelphians linalinganizidwa bwanji?
Pali makomiti osiyanasiyana amene amayangâanira ndi kuyendetsa ntchito ya umishonale, kuyangâanira ndi kuzonda odwala komanso okalamba, komanso anthu amene ali okhaokha. Komanso tili ndi maofesi mâmayiko angapo ndipo timafalitsa magazini ndi mabuku kudzera mâma ofesi amenewa. Koma tilibe anthu kapena atumiki amene alipidwa. Tilibenso bungwe limene tingati ndilamphamvu kapena limene limayangâanira gulu lathu. Ndalama zoyendetsera ntchito yathu yonse anthu a mâgulu la ma Christadelphians amachita kupereka okha popanda kuwakakamiza. Tilibenso ansembe.
Koma mwina mungafunse kuti: ngati palibe gulu loyendetsa ngulu limeneli, kodi nchito yonse ya ma Christadelpians imayenda bwanji? Yankho ndi lakuti izi zimatheka chifukwa choti tonse tili ndi chikhulupiriro chofanana komanso timachita zinthu zofanana. Zimenezi zimathandiza kuti tizichita zinthu mogwirizana komanso mokondana monga mamembala a gululi.
Gulu lililonse limakhala ndi dongosolo lawo loyendetsera zinth ndipo limasankha lokha âakuluâ otsogolera gululo. Izi zimachitika posankha akuluwo kamodzi chaka chilichonse mochita kuvota. Anthu amene amasankhidwa kuti azitumikira eklesia mâmautumiki osiyanasiyana, monga alembi, asungichuma, matcheyamani a misonkhano. Nâzoona kuti pali mâmadera ena amene mamembela a gululi amatha kupeza kapena kumanga nyumba zawozawo zopemphereramo. Komabe mâmadera ambiri amapempherera mânyumba ndi mâmaholo ochita kubwereka
Zikukhulupiriro zofanana
Ma Christadelphians, kulikonse kumene ali apadzikoli, akhala akuwerenga ndi kuphunzira mabuku awo opatulika ndipo akhala akukhulupirira zinthu zofanana. Patha zaka pafupifupi 100 tsopano pamene takhala ndi mawu a chikhulupiliro chathu. Tili ndi chikalata chotchedwa Chikalata cha Chikhulupiriro (chidule cha ziphunzitso za mâBaibulo) ndipo aliyese yemwe ndi membala amayensera kuchita zimenezi nthawi zonse kuti apitirize kukhala ndi chikhulupiriro chofanana ndi cha ma Christadelphian onse, chomwe ndi chochokera mâBaibulo. Zimenezi nâzimene zimatichititsa kuti tizigwirizana kwmbiri.
"Thupi limodzi . . . mzimu umodzi" (Aefeso 4:4-5)
Zimenezi zimachititsa kuti ma Christadelphians, kuli konse kumene ali, azitha kugwirizana komanso kusangalalira pamodzi.
Mtundu wa anthu amene tikuyesetsa kukhala
Tonsefe timafunika kuthandizidwa ndi Mulungu. Pa chifukwa chimenechi, timakhulupilira kuti ndi kofunika kwambiri kuti tidzipemphera. Chinthu chimodzi chimene timayesetsa kuchita tsiku ndi tsiku ndi kuwerenga Baibulo. Kuchita zimenezi nâkofunika kwambiri ngati mmene kulili kudya chakudya nthawi ndi nthawi. Kamodzi pa mlungu, timakumana ndi kudya mkate pangâono ndiponso kumwa vinyo pangâono pokumbukira imfa ya Ambuye wathu Yesu Khristu. Mudzapeza kuti ma Christadelphians ndi anthu osangalala chifukwa ali ndi chikhulupiliro chotsimikizika ndi zochita zawo. Popeza Yesu akubwera posachedwapa, tikufunika kukhala okonzeka. Izi zikutanthauza kukhala mâmoyo woyera ndi wokhulupirika. Zikutanthauzanso kupewa zinthu zonse zoipa. Ma Christadelphians ndi anthu omvera malamulo a dziko lawo. Amayesetsa kuchita zinthu zabwino momwe angathere, koma salowerera ndale, ndiponso samenya nkhondo kapena kutengera anthu kubwalo la milandu kuti akaweruzidwe. Amakhala ndi mkazi mâmodzi komanso amapewa chigololo. (Timazindikira kuti ena alipo kale amene ali ndi akazi opitilira mâmodzi pa nthawi imene iwo afika pakukhulupilira mawuwa, ndipo zoterezo zakambidwa mu Phunziro 33.)
Ma Christadelphian ali ndi Cholinga cha mâBaibulo
Ma CBM, monga mmene timatchulirana mwachidule, ntchito yathu ndi kuphunzitsa uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu mâdziko lonse lapansi. CBM imalengeza maphunziro, imalemba mabuku ndi zinthu zina zowerenga ndiponso imathandiza anthu kumvetsa Baibulo. CBM ili ndi anthu ogwira ntchito amene salipidwa malipiro alionse koma ndi a Christadelphian ongodzipereka kugwira ntchitoyi kuwonjezera pa ntchito imene amagwira yolembedwa ndi ena kumene amalandira malipiro. Cholinga chake ndi kuthandiza anthu kuphunzira uthenga wabwino, kuwalimbikitsa kulapa ndi kubatizidwa, ndiponso kuti adzitsatira chitsanzo cha Yesu ndi ophunzira ake.
Tikufuna kugawana nanu zikhulupiriro zathu, chiyembekezo chathu ndiponso chimwemwe chathu
Ma Christadelphian amakhulupilira kuti chikhulupiliro chawo nâchogwirizana ndi uthenga wabwino woona umene ukupezeka mâBaibulo lonse. Tikukhulupilira kuti inunso mudzasangalala kupeza Choonadi. Sikuti mudzangosangalala basi kuti mwapeza chinthu chabwino, koma mudzakhalanso ndi chiyembekezo, chisangalalo komanso chikondi. Mulungu akudalitseni pamene mukuyesetsa kufunafuna zinthu zimenezi.
Patsamba lotsatira pali mfundo zina zofunika kwambiri za mâBaibulo. Mavesi oyenera kuwerenga : Salmo 119:130; Mateyu 28:19-20; Yohane 17:3.
Lowezani : Yohane 15:13-14
"Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake. 14 Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulirani inu."
ZIPHUNZITSO ZINA ZOFUNIKA KWAMBIRI ZA MâBAIBULO
* Baibulo ndi uthenga woona wokhawo wochokera kwa Mulungu.
* Pali Mulungu mâmodzi yekha basi, Mlengi, amene amayendetsa zinthu padzikoli.
* Yesu Kristu ndi mwana wa Mulungu, wobadwa mwa Mariya. Anali munthu wosachimwa. Anafa imfa ya pa mtanda kupulumutsa iwo akukhulupilira iye. Anaukitsidwa kwa akufa ndipo pakali pano ali kumwamba.
* Posachedwapa Yesu adzabwera kuchokera kumwamba. Adzakhazikitsa Ufumu wa Mulungu pano padziko lapansi. Iye adzalamulira ngati Mfumu ndipo likulu lake lidzakhala Yerusalemu mâdziko la Israyeli.
* Ayuda ndi mboni za Mulungu pa cholinga chake, ngakhale ambiri mwa Ayudawo sadziwa zimenezi. Mulungu anapereka malonjezano kwa Abrahamu ndi kwa Davide amene adzakwaniritsidwa pakubwera kwakenso kwa Yesu pano padziko lapansi.
* Imfa ndi chilango cha uchimo ndipo anthu onse ndi ochimwa. Chiyembekezo cha moyo wina tikafa ndicho chiukiliro cha akufa Yesu akadzabwera.
* Padzakhala chiweruzo. Otsatira a Yesu onse okhulupirika adzapatsidwa moyo wosatha ndipo iwo adzathandiza iye kukonza mabvuto a dziko lapansi ndi kubweretsa mtendere ndi madalitso kwa mitundu yonse ya anthu.
* Tiyenera kukhulupilira uthenga wabwino, kulapa machimo athu ndi kubatizidwa. Ngati tiyesetsa kwambiri kutsatira malamulo a Mulungu, ndi kupemphera kuti atikhululukire tikalephera, tidzapulumutsidwa ndithu.
* Zimene Buku lopatulika lanenera zokhudza zinthu za kumbuyo ndi zinthu za nthawi yino zochitika mâdziko lapansi zaonekadi kuti zachitika. Zizindikiro zikuonetsa kuti Yesu Kristu watsala pangâono kubwera. Ndi chifukwa chache kuli kofunika kuti muyambe kuphunzira buku lopatulika panopa.
Christadelphian Bible Mission Box CBM, 404 Shaftmoor Lane, Birmingham B28 8SZ, England